damnlyrics.com

Wina Atikonda

Wina atikonda ife

Bwenzi lathu ndiyeyu

Atifunafuna ife

Inde nthawi zonsetu

Chorus: Chikondano chakechi

N’chachikulukuludi

Ndani mwa abale athu

Akanatifera ‘fe?

Koma Yesu m’malo mwathu;

Anapachikidwatu

Anam’nyosa pansi pano,

Bwenzi la ochimwawo

Enjoy the lyrics !!!